6 Ndipo ndakuonjezera pa masiku ako zaka khumi ndi zisanu; ndidzakupulumutsa iwe ndi mudzi uno m'dzanja la mfumu ya Asuri; ndidzacinjiriza mudzi uno, cifukwa ca Ine ndekha, ndi cifukwa ca Davide mtumiki wanga.
7 Nati Yesaya, Tenga ncinci yankhuyu. Naitenga, naiika papfundo, nacira iye.
8 Nati Hezekiya kwa Yesaya, Cizindikilo cace nciani kuti Yehova adzandiciza, ndi kuti ndidzakwera kumka ku nyumba ya Yehova tsiku lacitatu?
9 Nati Yesaya, Cizindikilo ndici akupatsa Yehova, kuti Yehova adzacicita conena iye; kodi mthunzi umuke m'tsogolo makwerero khumi, kapena ubwerere m'mbuyo makwerero khumi?
10 Nati Hezekiya, Kutsikira mthunzi makwerero khumi nkopepuka, kutero ai; koma mthunzi ubwerere makwerero khumi.
11 Napfuulirakwa Yehova Yesayamneneriyo, nabweza iye mthunzi m'mbuyo makwerero khumi, ndiwo amene udatsikira pa makwerero a Ahazi.
12 Nthawi ija Berodaki Baladani mwana wa Baladani mfumu ya Sabulo anatumiza akalata ndi mtulo kwa Hezekiya, popeza adamva kuti adadwala Hezekiya.