17 ndi Ahivi, ndi Aariki, ndi Asini;
18 ndi Aaravadi, ndi Aazemari, ndi Ahamati; pambuyo pace pamenepo ndipo mabanja a Akanani anafalikira.
19 Ndipo malire a Akanani anayamba pa Sidoni, pakunka ku Gerari ndi ku Gaza; pakunka ku Sodomu, ndi ku Gomora, ndi Adima, ndi Zeboimu, kufikira ku Lasa.
20 Amenewa ndi ana amuna a Hamu monga mwa mabanja ao, mwa zinenedwe zao, m'maiko ao, m'mitundu yao.
21 Ndiponso kwa Semu atate wa ana onse a Ebere, mkuru wa Yafeti, kwa iye kunabadwa ana.
22 Ana amuna a Semu; Elamu, ndi Ashuri, ndi Aripakasadi, ndi Ludi, ndi Aramu.
23 Ndi ana a Aramu: Uzi ndi Huli, ndi Getere, ndi Masi.