32 Ndipo Leyaanatenga pakati, nabala mwana wamwamuna, namucha dzina lace Rubeni; pakuti anati, Cifukwa kuti tsopano mwamuna wanga adzandikonda ine.
33 Ndipo anatenganso pakati, nabala mwana wamwamuna nati, Cifukwa anamva Yehova kuti anandida ine, anandipatsa ine mwana wamwamuna uyunso; ndipo anamucha dzina lace Simeoni.
34 Ndipo anatenganso pakati nabala mwana wamwamuna, nati, Tsopano lino mwamuna wanga adzadziphatika kwa ine cifukwa ndambalira iye ana amuna atatu; cifukwa cace anamucha dzina lace Levi.
35 Ndipo anatenganso pakati nabala mwana wamwamuna; nati, Tsopano ndidzamyamikira Yehova; cifukwa cace anamucha dzina lace Yuda; pamenepo analeka kubala.