4 Mbadwo wina opita, mbadwo wina nufika; koma dziko lingokhalabe masiku onse,
5 inde dzuwa lituruka, nililowa, nilifulumira komwe linaturukako.
6 Kulowa kumwela ndi kuzungulira: kumpoto zungulire zungulire imaomba mphepo; ibweranso monga mwa mazunguliridwe ace.
7 Mitsinje yonse ithira m'nyanja, koma nyanja yosadzala; komwe imukira mitsinjeyo, komweko ibweranso.
8 Zinthu zonse zilemetsa; munthu sakhoza kuzifotokoza; maso sakhuta m'kuona, ndi makutu sakhuta m'kumva.
9 Comwe cinaoneka cidzaonekanso; ndi comwe cinacitidwa cidzacitidwanso; ndipo palibe kanthu katsopano pansi pano.
10 Kodi pali kanthu unganene kuti, Taona katsopano aka? Kanalipo kale, kale lomwe tisanabadwe ife.