16 Pakuti monga ana a Yonadabu mwana wa Rekabu acita lamulo la kholo lao limene anawauza, koma anthu awa sanandimvera Ine.
17 Cifukwa cace atero Yehova, Mulungu wa makamu, Mulungu wa Israyeli: Taonani, ndidzafikitsa pa Yuda ndi pa onse okhala m'Yerusalemu coipa conseco ndawanenera iwo; cifukwa ndanena ndi iwo, koma sanamve; ndaitana, koma iwo sanandibvomera.
18 Ndipo Yeremiya anati kwa nyumba ya Arekabu, Atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli: Cifukwa mwamvera lamulo la Yonadabu kholo lanu, ndi kusunga zonse anakulangizani inu, ndi kucita monga mwa zonse anakuuzani inu;
19 cifukwa cace atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli: Yonadabu mwana wa Rekabu sadzasowa munthu wakuima pamaso panga kumuyaya.