8 Ndipo Akasidi adzabweranso, nadzamenyana ndi mudzi uwu; ndipo adzaulanda, nadzautentha ndi moto.
9 Yehova atero: Musadzinyenge, kuti, Akasidi adzaticokera ndithu; pakuti sadzacoka.
10 Pakuti ngakhale mukadakantha nkhondo yonse ya Akasidi akumenyana, nanu, ngakhale akadatsala olasidwa okha okha mwa iwo, koma iwowa akadauka yense m'hema wace ndi kutentha mudzi uwu ndi moto.
11 Ndipo panali pamene nkhondo ya Akasidi inacoka ku Yerusalemu cifukwa ca nkhondo ya Farao,
12 pamenepo Yeremiya anaturuka m'Yerusalemu kumuka ku dziko la Benjamini, kukalandira gawo lace kumeneko.
13 Pokhala iye m'cipinda ca Benjamini, kapitao wa alonda anali kumeneko, dzina lace Iriya, mwana wa Selemiya, mwana wa Hananiya; ndipo iye anamgwira Yeremiya mneneri, nati, Ulinkupandukira kwa Akasidi.
14 Ndipo anati Yeremiya, Kunama kumeneko; ine sindipandukira kwa Akasidi; koma sanamvera iye; ndipo Iriya anamgwira Yeremiya, nanka naye kwa akuru.