15 Onse opezedwa adzapyozedwa, ndi onse ogwidwa adzagwa ndi lupanga.
16 Makanda ao adzatswanyidwe pamaso pao; m'nyumba mwao mudzafunkhidwa, ndi akazi ao adzakakamizidwa.
17 Taonani, ndidzawautsira Amedi, amene sadzasamalira siliva, ngakhale golidi sadzakondwera naye.
18 Mauta ao adzatha anyamata; ndipo sadzacitira cisoni cipatso ca mimba; diso lao silidzaleka ana.
19 Ndipo Babulo, ulemerero wa maufumu, mudzi wokongolawo Akasidi anaunyadira, adzakhala monga momwe Mulungu anapasula Sodomu ndi Gomora.
20 Anthu sadzakhalamo konse, sadzakhalamo mbadwo ndi mbadwo; M-arabu sadzamanga hema wace pamenepo; abusa sadzagonetsa makamu ao kumeneko.
21 Koma zirombo za m'cipululu zidzagona pamenepo; nyumba zao zidzadzala ndi zakukuwa; ndipo nthiwatiwa zidzakhala pamenepo, ndipo atonde adzajidimuka pamenepo,