20 Ndipo mau a Yehova anadza nthawi yaciwiri kwa Hagai tsiku la makumi awiri la mwezi, ndi kuti,
21 Nena ndi Zerubabele ciwanga ca Yuda, kuti, Ndidzagwedeza miyamba ndi dziko lapansi;
22 ndipo ndidzagubuduza mipando yacifumu ya maufumu, ndidzaononga mphamvu ya maufumu a amitundu; ndidzagubuduza magareta ndi iwo akuyendapo; ndi akavalo ndi apakavalo adzatsika, yense ndi lupanga la mbale wace.
23 Tsiku lomwelo, ati Yehova wa makamu, ndidzakutenga, Zerubabele mtumiki wanga, mwana wa Sealitiyeli, ati Yehova, ndi kuika iwe ngati mphete yosindikizira; pakuti ndakusankha, ati Yehova wa makamu.