1 NDIPO mau a Yehova anadza kwa Yona mwana wa Amitai, ndi kuti,
2 Nyamuka, pita ku Nineve, mudzi waukuruwo, nulalikire motsutsana nao; pakuti coipa cao candikwerera pamaso panga.
3 Koma Yona ananyamuka kuti athawire ku Tarisi, kuzemba Yehova; ndipo anatsikira ku Yopa, napezako combo comuka ku Tarisi, napereka ndalama zace, natsikira m'menemo, kuti apite nao ku Tarisi kuzemba Yehova.
4 Koma Yehova anautsa cimphepo cacikuru panyanja, ndipo panali namondwe wamkuru panyanja, ndi combo cikadasweka.