3 Ndipo tsopano, Yehova, mundicotseretu moyo wanga, kundikomera ine kufa, osakhala ndi moyo ai.
4 Ndipo Yehova anati, Uyenera kupsa mtima kodi?
5 Pamenepo Yona anaturuka m'mudzi, nakhala pansi kum'mawa kwa mudzi, nadzimangira komweko thandala, nakhala pansi pace mumthunzi mpaka adzaona cocitikira mudzi.
6 Ndipo Yehova Mulungu anaikiratu msatsi, naumeretsera Yona, ucite mthunzi pamutu pace, kumlanditsa m'nsautso yace. Ndipo Yona anakondwera kwambiri cifukwa ca msatsiwo.
7 Koma Mulungu anauikira mphanzi pakuca m'mawa mwace, ndiyo inadya msatsi, nufota.
8 Ndipo kunali, poturuka dzuwa Mulungu anaika mphepo ya kum'mawa yotentha, ndipo dzuwa linatentha mutu wace wa Yona, nalefuka iye, nadzipempherera kuti afe; nati, Kundikomera ine kufa, kukhala ndi moyo ai.
9 Ndipo Mulungu anati kwa Yona, Uyenera kodi kupsa mtima cifukwa ca msatsiwo? Nati iye, Ee, kundiyenera ine kupsa mtima mpaka imfa.