9 pakuti mwa iye cikhalira cidzalo ca Umulungu m'thupi,
10 ndipo muli odzazidwa mwa iye, ndiye mutu wa ukulu wonse ndi ulamuliro;
11 amenenso munadulidwa mwa iye ndi mdulidwe wosacitika ndi manja, m'mabvulidwe a thupi, mu mdulidwe wa Kristu;
12 popeza munaikidwa m'manda pamodzi ndi iye muubatizo, momwemonso munaukitsidwa pamodzindi iye m'cikhulupiriro ca macitidwe a Mulungu, amene anamuukitsa iye kwa akufa.
13 Ndipo inu, pokhala akufa m'zolakwa ndi kusadulidwa kwa thupi lanu, anakupatsani moyo pamodzi ndi iye, m'mene adatikhululukira ife zolakwa zonse;
14 adatha kutifafanizira ca pa ifeco colembedwa m'zoikikazo, cimene cinali cotsutsana nafe; ndipo anacicotsera pakatipo, ndi kucikhomera ici pamtanda;
15 atabvula maukulu ndi maulamuliro, anawaonetsera poyera, nawagonjetsera nako.