22 Ndipo ena osinkhasinkha muwacitire cifundo,
23 koma ena 6 muwapulumutse ndi kuwakwatula kumoto; koma ena muwacitire cifundo ndi mantha, 7 nimudane naonso maraya ocitidwa mawanga ndi thupi
24 Ndipo 8 kwa iye amene akhoza kukudikirani mungakhumudwe, ndi 9 kukuimikani pamaso pa ulemerero wace opanda cirema m'kukondwera,
25 10 kwa Mulungu wayekha, Mpulumutsi wathu, mwa Yesu Kristu Ambuye wathu, zikhale ulemerero, ukulu, mphamvu, ndi ulamuliro zisanayambe nthawi, ndi tsopano, ndi kufikira nthawi zonse. Amen.