2 Imvani, mitundu ya anthu, inu nonse; tamvera, dziko lapansi, ndi zonse ziri m'mwemo; ndipo Ambuye Yehova akhale mboni yakutsutsa inu, Ambuye m'Kacisi wace wopatulika.
3 Pakuti, taonani, Yehova alikuturuka m'malo mwace, nadzatsika, nadzaponda pa misanje ya dziko lapansi.
4 Ndi mapiri adzasungunuka pansi pa Iye, ndi zigwa zidzang'ambika, ngati sera pamoto, ngati madzi otsanulidwa potsetseremba.
5 Cicitika ici conse cifukwa ca kulakwa kwa Yakobo, ndi macimo a nyumba ya Israyeli. Kulakwa kwa Yakobo nkotani? Si ndiko Samariya? ndi misanje ya Yuda ndi iti? si ndiyo Yerusalemu?
6 Cifukwa cace ndidzaika Samariya ngati mulu wa miyala ya m'munda, ngati zooka m'munda wamphesa; ndipo ndidzataya miyala yace m'cigwa, ndi kufukula maziko ace.
7 Ndi mafano ace osema onse adzaphwanyika, ndi mphotho zace zonse zidzatenthedwa ndi moto, ndi mafano ace onse ndidzawapasula; pakuti anazisonkhanitsa pa mphotho ya mkazi waciwerewere, ndipo zidzabwerera ku mphotho ya mkazi waciwerewere.
8 Cifukwa ca ici ndidzacita maliro, ndi kucema, ndidzayenda wolandidwa ndi wamarisece; ndidzalira ngati mimbulu, ndi kubuma ngati nthiwatiwa.