13 Cifukwa cace Inenso ndakukantha ndi kukupweteketsa; ndakupulula cifukwa ca zocimwa zako.
14 Udzadya koma osakhuta; ndi njala yako idzakhala pakati pako; ndipo udzacotsa koma osalanditsa; ndi ici wacilanditsa ndidzacipereka kulupanga.
15 Udzafesa koma osaceka; udzaponda azitona koma osadzola mafuta; udzaponda mphesa koma osamwa vinyo.
16 Pakuti asunga malemba a Omri, ndi nchito za nyumba ya Ahabu, ndipo mumayenda m'uphungu wao; kuti ndikusandulize bwinja, ndi okhalamo cotsonya; ndipo mudzasenza citonzo ca anthu anga.