7 Yehova ali wabwino, ndiye polimbikirapo tsiku la msauko; ndipo adziwa iwo omkhulupirira Iye.
8 Koma ndi cigumula cosefukira adzatha konse malo ace, nadzapitikitsira adani ace kumdima.
9 Mulingaliranji cotsutsana ndi Yehova? Iye adzatha psiti; nsautso siidzauka kawiri.
10 Pakuti cinkana akunga minga yoyangayanga, naledzera naco coledzeretsa cao, adzathedwa konse ngati ciputu couma.
11 Mwa iwe waturuka wina wolingalira coipa cotsutsana ndi Yehova, ndiye phungu wopanda pace.
12 Atero Yehova: Angakhale iwo ali ndi mphamvu yokwanira, nacuruka momwemo, koma momwemonso adzasalikidwa, ndipo iye adzapitiratu. Cinkana ndakuzunza iwe, sindidzakuzunzanso.
13 Koma tsopano ndidzatyola ndi kukucotsera goli lace, ndipo ndidzadula zomangira zako.