Nahumu 1 BL92

Cilungamo ndi cifundo ca Mulungu. Adzaononga adani ndi kulanditsa anthu ace

1 KATUNDU wa Nineve. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.

2 Yehova ndiye Mulungu wansanje, nabwezera cilango; Yehova ndiye wobwezera cilango, ndi waukali ndithu; Yehova ndiye wobwezera cilango oyambana naye, nasungira mkwiyo pa adani ace.

3 Yehova ndiye wolekerera mkwiyo, koma wa mphamvu yaikuru; ndi wosamasula ndithu woparamula; njira ya Yehova iri m'kabvumvulu ndi mumkuntho; ndipo mitambo ndiyo pfumbi la mapazi ace.

4 Adzudzula nyanja, naiphwetsa, naumitsa mitsinje yonse; Basana ndi Karimeli afota, ndi duwa la ku Lebano linyala.

5 Mapiri agwedezeka cifukwa ca Iye, ndi zitunda zisungunuka; ndi dziko lapansi likwezeka pamaso pace, ndi maiko ndi onse okhala m'mwemo.

6 Adzaima ndani pa kulunda kwace? ndipo adzakhalitsa ndani pa mkwiyo wace wotentha? ukali wace utsanulidwa ngati moto, ndi matanthwe asweka ndi Iye.

7 Yehova ali wabwino, ndiye polimbikirapo tsiku la msauko; ndipo adziwa iwo omkhulupirira Iye.

8 Koma ndi cigumula cosefukira adzatha konse malo ace, nadzapitikitsira adani ace kumdima.

9 Mulingaliranji cotsutsana ndi Yehova? Iye adzatha psiti; nsautso siidzauka kawiri.

10 Pakuti cinkana akunga minga yoyangayanga, naledzera naco coledzeretsa cao, adzathedwa konse ngati ciputu couma.

11 Mwa iwe waturuka wina wolingalira coipa cotsutsana ndi Yehova, ndiye phungu wopanda pace.

12 Atero Yehova: Angakhale iwo ali ndi mphamvu yokwanira, nacuruka momwemo, koma momwemonso adzasalikidwa, ndipo iye adzapitiratu. Cinkana ndakuzunza iwe, sindidzakuzunzanso.

13 Koma tsopano ndidzatyola ndi kukucotsera goli lace, ndipo ndidzadula zomangira zako.

14 Ndipo Yehova walamulira za iwe kuti asabzalidwenso ena a dzina lako; m'nyumba ya milungu yako ndidzacotsa fano losema ndi fano loyenga; ndidzakukonzerapo manda, pakuti iwe ndiwe wopepuka.

15 Taonani pamapiri mapazi a iye wakulalikira uthenga wabwino, wakubukitsa mtendere! cita madyerero ako, Yuda, kwaniritsa zowinda zako; pakuti wopanda paceyo sadzapitanso mwa iwe; iye waonongeka konse.

Mitu

1 2 3