Nahumu 2 BL92

Nineve amangidwa misasa nalandidwa

1 Wophwanyayo wakwera pamaso pako; sunga linga, yang'anira panjira, limbitsa m'cuuno mwako, limbikitsatu mphamvu yako.

2 Pakuti Yehova abwezeranso ukulu wace wa Yakobo ngati ukulu wace wa Israyeli; pakuti okhuthula anawakhuthula, naipsa nthambi zace za mpesa.

3 Zikopa za amphamvu ace zasanduka zofiira, ngwazi zibvala mlangali; magareta anyezimira ndi citsulo tsiku la kukonzera kwace, ndi mikondo itinthidwa.

4 Magareta acita mkokomo m'miseu, akankhana m'makwalala; maonekedwe ao akunga miuni, athamanga ngati mphezi.

5 Akumbukila omveka ace; akhumudwa m'kupita kwao, afulumira ku linga lace, ndi cocinjiriza cakonzeka.

6 Pa zipata za mitsinje patseguka, ndi cinyumba casungunuka.

7 Catsimikizika, abvulidwa, atengedwa, adzakazi ace alira ngati mau a nkhunda, nadziguguda pacifuwa pao.

8 Koma Nineve wakhala ciyambire cace ngati thamanda lamadzi; koma athawa. Imani, Imani! ati, koma palibe woceuka.

9 Funkhani siliva, funkhani golidi; pakuti palibe kutha kwace kwa zosungikazo, kwa cuma ca zipangizo zofunika ziri zonse.

10 Ndiye mopanda kanthu mwacemo ndi mwacabe, ndi wopasuka; ndi mtima usungunuka, ndi maondo aombana, ndi m'zuuno zonse muwawa, ndi nkhope zao zatumbuluka.

11 Iri kuti ngaka ya mikango, ndi podyera misona ya mikango; kumene mkango, waumuna ndi waukazi, ukayenda ndi mwana wa mkango, kopanda wakuiposa?

12 Mkangowo unamwetula zofikira ana ace, nusamira yaikazi yace, nudzaza mapanga ace ndi nyama, ngaka zace ndi zojiwa.

13 Taona, nditsutsana nawe, ati Yehova wa makamu, ndipo ndidzatentha magareta ace m'utsi; ndi lupanga lidzadya misona yako ya mkango; ndipo ndidzacotsa zofunkha zako pa dziko lapansi, ndi mau a mithenga yako sadzamvekanso.

Mitu

1 2 3