1 Wophwanyayo wakwera pamaso pako; sunga linga, yang'anira panjira, limbitsa m'cuuno mwako, limbikitsatu mphamvu yako.
2 Pakuti Yehova abwezeranso ukulu wace wa Yakobo ngati ukulu wace wa Israyeli; pakuti okhuthula anawakhuthula, naipsa nthambi zace za mpesa.
3 Zikopa za amphamvu ace zasanduka zofiira, ngwazi zibvala mlangali; magareta anyezimira ndi citsulo tsiku la kukonzera kwace, ndi mikondo itinthidwa.
4 Magareta acita mkokomo m'miseu, akankhana m'makwalala; maonekedwe ao akunga miuni, athamanga ngati mphezi.