2 Kumveka kwa cikoti, ndi mkokomo wa kuyenda kwa njinga za magareta; ndi kaphata kaphata wa akavalo, ndi gwegwegwe wa magareta;
3 munthu wokwera pa kavalo, ndi lupanga lonyezimira, ndi mkondo wong'anipa; ndi aunyinji ophedwa, ndi cimulu ca mitembo, palibe kutha zitanda; angokhumudwa ndi zitanda;
4 cifukwa ca ciwerewere cocuruka ca waciwerewere wokongola, ndiye mkaziyo mwini nyanga, wakugulitsa amitundu mwa ciwerewere cace, ndi mabanja mwa nyanga zace.
5 Taona, nditsutsana nawe, ati Yehova wa makamu, ndidzaphimba nkhope yako ndi nsaru yako yoyesa mthendene; ndipo ndidzaonetsa amitundu umarisece wako, ndi maufumu manyazi ako.
6 Ndipo ndidzakuponyera zonyansa, ndi kukucititsa manyazi, ndi kukuika copenyapo,
7 Ndipo kudzali kuti onse akupenyerera iwe adzakuthawa, nadzati, Nineve wapasuka, adzamlira maliro ndani? ndidzakufunira kuti akukutonthoza?
8 Kodi uli wabwino woposa No-Amoni, wokhala pakati pa mitsinje wozingidwa ndi madzi; amene chemba lace ndilo nyanja, ndi linga lace ndilo nyanja?