1 Tsoka uyo wopanduka, ndi wodetsedwa, ndiye mudzi wozunza!
2 Sanamvera mau, sanalola kulangizidwa; sanakhulupirira Yehova, sanayandikira kwa Mulungu wace.
3 Akalonga ace m'kati mwace ndiwo mikango yobangula; oweruza ace ndi mimbulu ya madzulo, sasiya kanthu ka mawa.
4 Aneneri ace ndiwo anthu a matukutuku ndi onyenga; ansembe ao anaipsa malo opatulika, napotoza cilamulo.