9 Pakuti Mulungu sanatiika ife tilawe mkwiyo, komatu kuti tilandire cipulumutso mwa Ambuye wathu Yesu Kristu,
10 amene anafa m'malo mwathu, kuti, tingakhale tidikira, tingakhale tigona, tikakhale ndi moyo pamodzi ndi Iye.
11 Mwa ici cenjezanani, ndipo mangiriranani wina ndi mnzace, monganso mumacita,
12 Koma, abale, tikupemphani, dziwani iwo akugwiritsa nchito mwa inu, nakhala akulu anu mwa Ambuye, nakuyatnbirirani inu;
13 ndipo muwacitire ulemu woposatu mwa cikondi, cifukwa ca nchito yao. Khalani mumtendere mwa inu nokha.
14 Koma tidandaulira inu abale, yambirirani ampwayi, limbikitsani amantha mtima? cirikizani ofok a, mukhale oleza mtima pa onse.
15 Penyani kuti wina asabwezere coipa womcitira coipa; komatu nthawi zonse mutsatire cokoma, kwa anzanu, ndi kwa onse.