1 Koma zindikira ici, kuti masiku otsiriza zidzafika nthawi zowawitsa.
2 Pakuti anthu adzakhala odzikonda okha, okonda ndarama, odzitamandira, odzikuza, amwano, osamvera akuwabala, osayamika,
3 osayera mtima, opanda cikondi cacibadwidwe, osayanjanitsika, akudierekeza, osakhoza kudziletsa, aukali, osakonda abwino,
4 aciwembu, aliuma olimbirira, otukumuka mtima, okonda zokondweretsa munthu, osati okonda Mulungu;
5 akukhala nao maonekedwe a cipembedzo, koma mphamvu yace adaikana; kwa iwonso udzipatule,
6 Pakuti mwa iwo akhala akukwawira m'nyumba, nagwira akazi opusa, osenza akatundu a zoipa zao, otengedwa nazo zilakolako za mitundu mitundu: