7 Ndalimbana nako kulimbana kwabwino, ndatsiriza njirayo, ndasunga cikhulupiriro:
8 cotsalira wandiikira ine korona wa cilungamo, amene Ambuye, woweruza wolungama, adzandipatsa ine tsiku lijalo: ndipo si kwa ine ndekha, komatunso kwa onse amene anakonda maonekedwe ace.
9 Tayesetsa kudza kwa ine msanga:
10 pakuti Dema wandisiya ine, atakonda dziko lino lapansi, napita ku Tesalonika; Kresike ku Galatiya, Tito ku Dalimatiya.
11 Luka yekha ali pamodzi ndi ine. Umtenge Marko, adze pamodzi ndi iwe; pakuti ayenera kunditumikira.
12 Koma Tukiko ndamtuma ku Efeso.
13 Copfunda cija ndinacisiya ku Trowa kwa Karpo, udze naco pakudza iwe, ndi mabuku, makamaka zikopa zija zolembedwa.