12 Koma abale, ndifuna kuti muzindikire kuti zija za kwa ine zidacita makamaka kuthandizira Uthenga Wabwino;
13 kotero kuti zomangira zanga zinaonekera mwa Kristu m'bwalo lonse da alonda, ndi kwa onse ena;
14 ndi kuti unyinji wa abale mwa Ambuye, pokhulupirira m'zomangira zanga, alimbika mtima koposa kulankhula mau a Mulungu opanda mantha.
15 Enatu alalikiranso Kristu cifukwa ca kaduka ndi ndeu; koma enanso cifukwa ca kukoma mtima;
16 ena atero ndi cikondi, podziwa kuti anandiika ndicite eokanira ca Uthenga Wabwino;
17 koma ena alalikira Kristu mocokera m'cotetana, kosati koona, akuyesa kuti adzandibukitsira cisautso m'zomangira zanga.
18 Potero nciani? Cokhaco kuti monsemo, ngati pamaso pokha, ngati m'coonadi, Kristu alalikidwa; ndipo m'menemo ndikondwera, komanso ndidzakondwera.