3 musacite kanthu monga mwa cotetana, kapena monga mwa ulemerero wopanda pace, komatu ndi kudzicepetsa mtima, yense ayese anzace omposa iye mwini;
4 munthu yense asapenyerere zace za iye yekha, koma yense apenyererenso za mnzaceo
5 Mukhale nao mtima m'kati mwanu umene unalinso mwa Kristu Yesu,
6 ameneyo, pokhala nao maonekedwe a Mulungu, sanaciyesa colanda kukhala wofana ndi Mulungu,
7 koma anadzikhuthula yekha, natenga maonekedwe akapolo, nakhala m'mafanizidwe a anthu;
8 ndipo popezedwa m'maonekedwe ngati munthu, anadzicepetsa yekha, nakhala womvera kufikira imfa, ndiyo imfa ya pamtanda.
9 Mwa icinso Mulungu anamkwezetsa iye, nampatsa dzina limene liposa maina onse,