18 Pakuti ambiri amayenda, za amene ndinakuuzani kawiri kawiri, ndipo tsopanonso ndikuuzani ndi kulira, ali adani a mtanda wa Kristu;
19 citsiriziro cao ndico kuonongeka, mulungu wao ndiyo niimba yao, ulemerero wao uli m'manyazi ao, amenealingirira za padziko.
20 Pakuti ufulu wathu uli Kumwamba; z kucokera komwenso tilindirira Mpulumutsi, Ambuye Yesu Kristu;
21 amene adzasanduliza thupi lathu lopepulidwa, lifanane nalo thupi lace la ulemerero, monga mwa macitidwe amene akhoza kudzigonjetsera nao zinthu zonse.