1 Cifukwa cace ngati munaukitsidwa pamodzi ndi Kristu, funani zakumwamba, kumene kuli Kristu wokhala pa dzanja lamanja la Mulungu.
2 Lingalirani zakumwamba osati za padziko ai.
3 Pakuti munafa, ndipo moyo wanu wabisika pamodzi ndi Kristu mwa Mulungu,
4 Pamene Kristu adzaoneka, ndiye moyo wathu, pamenepo inunso mudzaonekera pamodzi ndi iye m'ulemerero.