13 Umboni uwu uli woona. Mwa ici uwadzudzule mokaripa, kuti akakhale olama m'cikhulupiriro,
14 osasamala nthanu zacabe za Ciyuda, ndi malamulo a anthu opatuka kusiyana naco coonadi.
15 Zonse ziyera kwa iwo amene ayera mtima; koma kwa iwo odetsedwa ndi osakhulupira kulibe kanthu koyera; komatu zadetsedwa nzeru zao ndi cikumbu mtima cao.
16 Abvomereza kuti adziwa Mulungu, koma ndi Debito zao amkana iye, popeza ali onyansitsa, ndi osamvera, ndi pa nchito zonse zabwino osatsimikizidwa.