Tito 3 BL92

1 Uwakumbutse iwo agonje kwa akulu, ndi aulamuliro, akhale omvera, okonzeka pa nchito iri yonse yabwino;

2 asacitire mwano munthu ali yense, asakhale andeu, akhale aulere, naonetsere cifatso conse pa anthu onse.

3 Pakuti kale ifenso tinali opusa, osamvera, onyengeka, akucitira ukapolo zilakolako ndi zokondweretsa za mitundu mitundu, okhala m'dumbo ndi njiru, odanidwa, odana wina ndi mnzace.

4 Koma pamene kukoma mtima, ndi cikondi ca pa anthu, ca Mpulumutsi wathu Mulungu zidaoneka,

5 zosati zocokera m'nchito za m'cilungamo, zimene tidazicita ife, komatu monga mwa cifundo cace anatipulumutsa ife, mwa kutsuka kwa kubadwanso ndi makonzedwe a Mzimu Woyera,

6 amene anatsanulira pa ife mocurukira, mwa Yesu Kristu Mpulumutsi wathu;

7 kuti poyesedwa olungama ndi cisomo ca Iyetu, tikayesedwe olowa nyumba monga mwa ciyembekezo ca moyo wosatha.

8 Okhulupirika mauwa, ndipo za izi ndifuna kuti ulimbitse mau, kuti iwo akukhulupirira Mulungu asamalire akhalebe atsogoleri a nchito zabwino. Izi nzokoma ndi zopindulitsa anthu;

9 koma pewa mafunso opusa, ndi mawerengedwe a mibadwo, ndi ndeu, ndi makani a pamalamulo; pakuti sizipindulitsa, ndipo ziri zacabe.

10 Munthu wopatukira cikhulupiriro, utamcenjeza kamodzi ndi kawiri, umkanize,

11 podziwa kuti worereyo wasandulika konse, nacimwa, nakhala wodzitsutsa Yekha.

12 Pamene ndikatuma Artema kwa iwe, kapena Tukiko, cita cangu kudza kwa ine ku Nikopoli: pakuti ndatsimikiza mtima kugonerako nyengo yacisanu.

13 Zena nkhoswe ya mirandu, ndi Apolo ufulumire kuwakonzera zaulendo, kuti asasowe kanthu,

14 Ndipo anthu athu aphunzirenso asunge nchito zabwino zofunika, kuti asakhale osabala zipstso.

15 Akulankhula iwe onse akukhala pamodzi ndi ine. Lankhula otikondawo m'cikhulupiriro.Cisomo cikhale ndi inu nonse.

Mitu

1 2 3