11 Iwenso udzaledzera, udzabisala; iwenso udzafunanso polimbikira cifukwa ca mdani.
12 Malinga ako onse adzanga mikuyu ndi nkhuyu zoyamba kupsa; akaigwedeza zingokugwa m'kamwa mwa wakudya.
13 Taona, anthuako m'kati mwako akunga akazi; zipata za dziko lako zatsegulidwira adani ako papakuru; moto watha mipingiridzo yako.
14 Udzitungiretu madzi a nthawi yokumangira misasa, limbikitsa malinga ako, lowa kuthope, ponda dothi, limbitsa ng'anjo yanjerwa.
15 Pomwepo moto udzatha iwe; lupanga lidzakuononga; lidzatha iwe ngati cirimamine; udzicurukitse ngati cirimamine, udzicurukitse ngati dzombe.
16 Wacurukitsa amalonda ako koposa nyenyezi za kuthambo; cirimamine anyambita, nauluka, nathawa.
17 Obvala korona ako akunga dzombe, ndi akazembe, ndi akazembe ako ngati ziwalamsatsi zakutera m'macinga tsiku lacisanu, koma likafundukula dzuwa ziuluka nizithawa, ndi kumene zinakhalako sikudziwikanso.