6 Ndipo ndidzakuponyera zonyansa, ndi kukucititsa manyazi, ndi kukuika copenyapo,
7 Ndipo kudzali kuti onse akupenyerera iwe adzakuthawa, nadzati, Nineve wapasuka, adzamlira maliro ndani? ndidzakufunira kuti akukutonthoza?
8 Kodi uli wabwino woposa No-Amoni, wokhala pakati pa mitsinje wozingidwa ndi madzi; amene chemba lace ndilo nyanja, ndi linga lace ndilo nyanja?
9 Kusi ndi Aigupto ndiwo mphamvu yace, ndiyo yosatha, Puti ndi Lubimu ndiwo akukuthandiza.
10 Koma iye anatengedwa, analowa ndende; ana ace a makanda anaphwanyika polekeza pace pa miseu yace yonse; ndi pa omveka ace anacita maere, ndi akulu ace onse anamangidwa maunyolo.
11 Iwenso udzaledzera, udzabisala; iwenso udzafunanso polimbikira cifukwa ca mdani.
12 Malinga ako onse adzanga mikuyu ndi nkhuyu zoyamba kupsa; akaigwedeza zingokugwa m'kamwa mwa wakudya.