1 MAU a Yehova a kwa Yoeli mwana wa Petueli.
2 Imvani ici, akulu akulu inu, nimuchere khutu, inu nonse okhala m'dziko. Cacitika ici masiku anu kodi, kapena masiku a makolo anu?
3 Mufotokozere ana anu ici, ndi ana anu afotokozere ana ao, ndi ana ao afotokozere mbadwo wina.
4 Cosiya cimbalanga, dzombe lidacidya; ndi cosiya dzombe, cirimamine adacidya; ndi cosiya cirimamine, anoni adacidya.