3 Moto unyambita pamaso pao, ndi m'mbuyo mwao litentha lawi la moto; kumaso kwao dziko likunga munda wa Edeni, koma m'mbuyo mwao likunga cipululu copanda kanthu; palibenso wakuwapulumuka.
4 Maonekedwe ao aoneka ngati akavalo, nathamanga ngati akavalo a nkhondo.
5 Atumphako ngati mkokomo wa magareta pamwamba pa mapiri, ngati kulilima kwa malawi a moto akupsereza ziputu, ngati mtundu wamphamvu wa anthu ondandalikira nkhondo.
6 Pamaso pao mitundu ya anthu ikumva zowawa, nkhope zonse zitumbuluka.
7 Athamanga ngati amphamvu; akwera linga ngati anthu a nkhondo; niliyenda liri lonse njira yace, osasokonezeka m'mabande ao.
8 Sakankhana, ayenda liri lonse m'mopita mwace; akagwa m'zida, siityoka nkhondo yao.
9 Alumphira mudzi, athamanga palinga, akwerera nyumba, alowera pamazenera ngati mkhungu.