18 Ndipo kudzacitika tsiku ilo mapiri adzakhetsa vinyo wozuna, ndi pazitunda padzayenda mkaka, ndi m'mitsinje yonse ya Yuda mudzayenda madzi; ndi madzi a kasupe adzaturuka m'nyumba ya Yehova, nadzamwetsa madzi cigwa ca Sitimu.
19 Aigupto adzasanduka bwinja, ndi Edomu adzasanduka cipululu copanda kanthu, cifukwa ca ciwawaci anawacitira ana a Yuda; popeza anakhetsa mwazi wosacimwa m'dziko lao.
20 Koma Yuda adzakhala cikhalire, ndi Yerusalemu ku mibadwo mibadwo.
21 Ndipo ndidzayeretsa mwazi wao umene sindinauyeretsa, pakuti Yehova akhala m'Ziyoni.