18 podziwa kuti simunaomboledwa ndi zobvunda, golidi ndi siliva, kusiyana nao makhalidwe anu acabe ocokera kwa makolo anu:
19 koma 1 ndi mwazi wa mtengo wace wapatali 2 monga wa mwana wa nkhosa wopanda cirema, ndi wopanda banga, ndiwo mwazi wa Kristu:
20 3 amene anazindikirikatu lisanakhazikike dziko lapansi, koma anaonetsedwa pa citsiriziro ca nthawi,
21 cifukwa ca inu amene mwa rye mukhulupirira Mulungu 4 wakwnuukitsa iye kwa akufa, ndi kumpatsa iye ulemerero; kotero kuti cikhulupiriro canu ndi ciyembekezo canu cikhale pa Mulungu.
22 Popeza 5 mwayeretsa moyo wanu pakumvera coonadi kuti 6 mukakonde abale ndi cikondi cosanyenga, mukondane kweni kweni kucokera kumtima;
23 7 inu amene mudabadwanso, osati ndi mbeu yofeka, komatu yosaola, mwa mau a Mulungu amoyo ndi okhalitsa.
24 Popeza,8 Anthu onse akunga udzu,Ndi ulemerero waowonse ngad duwa la udzu.Udzuwo ungotota, ndi duwa lace lingogwa;