5 inunso ngati miyala yamoyo mumangidwa nyumba ya uzimu, kun mukhale ansembe oyera mtima, akupereka nsembe zauzimu, zolandiridwa ndi Mulungu mwa Yesu Kristu,
6 Cifukwa kwalembedwa m'lembo,Taona, ndiika m'Ziyoni mwala wotsiriza wa pangondya, wosankhika, wa mtengo wace;Ndipo wokhulupirira iye sadzanyazitsidwa.
7 Kwa inu tsono akukhulupira, ali wa mtengo wace; koma kwa iwo osakhulupira,Mwala umene omangawo anaukana,Womwewo unayesedwa mutu wa pangondya;
8 ndipo,Mwala wakukhumudwa nao, ndi thanthwe lopunthwitsa;kwa iwo akukhumudwa ndi mau, pokhala osamvera, kumenekonso adaikidwako.
9 Koma inu ndinu mbadwa yosankhika, ansembe acifumu, mtundu woyera mtima, anthu a mw ni wace, kotero kuti mukalakire zoposazo za iye amene anakuitanani muturuke mumdima, mulowe kuunika kwace kodabwitsa;
10 inu amene kale simunali anthu, koma tsopano muli anthu a Mulungu; amene kale simunalandira cifundo, koma tsopano mwalandira cifundo.
11 Okondedwa, ndikudandaulirani ngati alendo ndi ogonera mudzikanize zilakolako za thupi zimene zicita nkhondo pa moyo;