2 pakuona mayendedwe anu oyera ndi kuopa kwanu.
3 Amene kukometsera kwanu kusakhale kwa kunja, kuluka tsitsi ndi kubvala za golidi, kapena kubvala cobvala;
4 koma kukhale munthu wobisika wamtima, m'cobvala cosaola ca mzimu wofatsa ndi wacete, ndiwo wa mtengo wace wapatali pamaso pa Mulungu.
5 Pakuti koteronso kale akazi oyera mtima, akuyembekezera Mulungu, anadzikometsera okha, namvera amuna ao a iwo okha;
6 monga Sara anamvera Abrahamu, namucha iye mbuye; ameneyo mukhala ana ace ngati mucita bwino, osaopa coopsa ciri conse.
7 Momwemonso amuna inu, khalani nao monga mwa cidziwitso, ndi kucitira mkazi ulemu, monga cotengera cocepa mphamvu, monganso wolowa nyumba pamodzi wa cisomo ca moyo, kuti mapemphero anu angaletsedwe.
8 Cotsalira, khalani nonse a mdma umodzi, ocitirana cifundo, okondana ndi abale, acisoni, odzicepetsa: