4 mwa izi adatipatsa malonjezano a mtengo wace ndi akuru ndithu; kuti mwa izi mukakhale oyanjana nao umulungu wace, mutapulumuka ku cibvundi ciri pa dziko lapansi m'cilakolako.
5 Ndipo mwa ici comwe, pakutengeraponso cangu conse, muonjezerapo ukoma pa cikhulupiriro canu, ndi paukoma cizindikiritso; ndi pacizindikiritso codziletsa;
6 ndi pacodziletsa cipiriro;
7 ndi pacipiriro zipembedzo; ndi pactpembedzo cikondi ca pa abale; ndi pacikondi ca pa abale cikondi.
8 Pakuti izi zikakhala ndi inu, ndipo zikacuruka, zidzacita kuti musakhale aulesi kapena opanda zipatso pa cizindikiritso ca Ambuye wathu Yesu Kristu.
9 Pakuti iye wakusowa izi ali wakhungu, wa cimbuuzi, woiwala matsukidwe ace potaya zoipa zace zakale,
10 Momwemo abale, onjezani kucita cangu kukhazikitsa maitanidwe ndi masankhulidwe anu; pakuti mukacita izi, simudzakhumudwa nthawi zonse;