26 popeza anali wolakalaka inu nonse, nabvutika mtima cifukwa mudamva kuti anadwala.
27 Pakutinso anadwaladi pafupi imfa; komatu Mulungu anamcitira cifundo; koma si iye yekha, komatu inenso, kuti ndisakhale naco cisoni cionjezere-onjezere.
28 Cifukwa cace ndamtuma iye cifulumizire, kuti pakumuona mukakondwerenso, ndi inenso cindicepere cisoni.
29 Cifukwa cace mumlandire mwa Ambuye, ndi cimwemweconse; nimucitire ulemu oterewa;
30 pakuti cifukwa lea nchito ya Kristu anafikira pafupi imfa, wosasamalira moyo wace, kuti z akakwaniritse ciperewero ca utumiki wanu wa kwa ine.