9 Ndidzasenza mkwiyo wa Yehova, cifukwa ndamcimwira, mpaka andinenera mlandu wanga, ndi kundiweruzira mlandu wanga; adzanditurutsira kwa kuunika, ndipo ndidzapenya cilungamo cace.
10 Pamenepo mdani wanga adzaciona, ndi manyazi adzamkuta iye amene adati kwa ine, Ali kuti Yehova Mulungu wako? Maso anga adzamuona; tsopano adzampondereza ngati thope la m'miseu.
11 Tsiku lakumanga malinga ako, tsiku lomwelo lembalo lidzacotsedwa kunka kutali.
12 Tsiku lomwelo adzadza kwa iwe, kucokera ku Asuri ndi midzi ya ku Aigupto, kuyambira ku Aigupto kufikira ku Mtsinje, ndi kuyambira kunyanja kufikira kunyanja, ndi kuyambira kuphiri kufikira kuphiri.
13 Koma dziko lidzakhala labwinja cifukwa ca iwo okhalamo, mwa zipatso za macitidwe ao.
14 Mudyetse anthu anu ndi ndodo yanu, nkhosa za colowa canu zokhala pa zokha m'nkhalango pakati pa Karimeli, zidye m'Basana ndi m'Gileadi masiku a kale lomwe.
15 Monga masiku a kuturuka kwako m'dziko la Aigupto ndidzamuonetsa zodabwitsa.