1 Akulu tsono mwa inu ndiwadandaulira, ine mkulu mnzanu ndi mboni ya zowawa za Kristu, ndinenso wolawana nao ulemerero udzabvumbulutsikawo:
2 Wetani gulu la Mulungu liri mwa inu, ndi kuliyang'anira, osati mokangamiza, koma mwaufulu, kwa Mulungu; osatsata phindu lonyansa, koma mwacangu;
3 osati monga ocita ufumu pa iwo a udindo wanu, koma okhala zitsanzo za gululo.
4 Ndipo pakuonekera Mbusa wamkulu, mudzalandira korona wa ulemerero, wosafota. Momwemonso, anyamata inu, mverani akulu.
5 Koma nonsenu mubvale kudzicepetsa kuti mutumikirane; pakuti Mulungu akaniza odzikuza, koma apatsa cisomo kwa odzicepetsa.
6 Potero dzicepetseni pansi pa dzanja la mphamvu lao Mulungu, kuti panthawi yace akakukwezeni;
7 ndi kutaya pa iye nkhawa yanu yonse, pakuti iye asamalira inu.