1 Cifukwa ca ici ine Paulo, ndine wandende wa Kristu Yesu cifukwa ca inu amitundu,
2 ngatitu munamva za udindo wa cisomo ca Mulungucimene anandipatsa ine ca kwa inu;
3 ndi umo anandizindikiritsa cinsinsico mwa bvumbulutso, monga ndinalemba kale mwacidule,
4 cimene mukhoza kuzindikira naco, pakuciwerenga, cidziwitso canga m'cinsinsi ca Kristu,