14 Cifukwa ca ici ndipinda maondo anga kwa Atate,
15 amene kucokera kwa iye pfuko lonse la m'mwamba ndi la padziko alicha dzina,
16 kuti monga mwa cuma ca ulemerero wace akulimbikitseni inu ndi mphamvu mwa Mzimu wace, m'kati mwanu,
17 kuti Kristu akhale cikhalire mwa cikhulupiriro m'mitima yanu; kuti, ozika mizu ndi otsendereka m'cikondi,
18 mukakhozetu kuzindikira pamodzi ndi oyera mtima onse, kupingasa, ndi utali, ndi kukwera,
19 ndi kuzama nciani; ndi kuzindikira cikondi ca Kristu, cakuposa mazindikiridwe, kuti mukadzazidwe kufikira cidzalo conse ca Mulungu.
20 Ndipo kwa iye amene angathe kucita koposa-posatu zonse zimene tizipempha, kapena tiziganiza, monga mwa mphamvu ya kucita mwa ife,