25 Mwa ici, mutataya zonama, 3 lankhulani zoona yense ndi mnzace; 4 pakuti tiri ziwalo wina ndi mnzace.
26 5 Kwiyani, koma musacimwe; dzuwa lisalowe muli cikwiyire,
27 ndiponso 6 musampatse malo mdierekezi.
28 Wakubayo asabenso; koma 7 makamaka agwiritse nchito, nagwire nchito yokoma ndi manja ace, kuti akhale naco cakucereza wosowa.
29 8 Nkhani yonse yobvunda isaturuke m'kamwa mwanu, koma ngati pali yina yabwino kukumangirira monga mofunika ndiyo, 9 kuti ipatse cisomo kwa iwo akumva.
30 Ndipo 10 musamvetse cisoni Mzimu Woyera wa Mulungu, amene munasindikizidwa cizindikilo mwa iye, kufikira tsiku la maomboledwe.
31 11 Ciwawo conse, ndi kupsya mtima, ndi mkwiyo, ndi ciwawa, ndi mwano zicotsedwe kwa inu, ndiponso coipa conse.