17 Cifukwa cace musakhale opusa, koma dziwitsani cifuniro ca Ambuye nciani.
18 Ndipo musaledzere naye vinyo, m'mene muli citayiko; komatu mudzale naye Mzimu,
19 ndi kudzilankhulira nokha ndi masalmo, ndi mayamiko, ndi nyimbo zauzimu, kuyimbira ndi kuyimba m'malimba Ambuye mumtima mwanu;
20 ndi kuyamika Mulungu Atate masiku onse, cifukwa ca zonse, m'dzina la Ambuye wathu Yesu Kristu;
21 ndi kumverana wina ndi mnzace m'kuopa Kristu.
22 Akazi Inu, mverani amuna anu ainu eni, monga kumvera Ambuye.
23 Pakuti mwamuna ndiye mutu wa mkazi, monganso Kristu ndiye mutu wa Eklesia, ali yekha Mpulumutsi wa thupilo.