1 PAULO, mtumwi (wosacokera kwa anthu, kapena mwa munthu, koma mwa Yesu Kristu, ndi Mulungu Atate, amene anamuukitsa iye kwa akufa),
2 ndi abale onse amene ali pamodzi ndi ine, kwa Mipingo ya ku Galatiya:
3 Cisomo kwa inu, ndi mtendere wa kwa Mulungu Atate, ndi Ambuye wathu Yesu Kristu,
4 amene anadzipereka yekha cifukwa ca macimo athu, kuti akatilanditse ife m'nyengo ya pansi pano yino yoipa, monga mwa cifuniro ca Mulungu ndi Atate wathu;
5 yemweyo akhale nao ulemerero ku nthawi za nthawi. Amen.