20 Ndipo izi ndikulemberani inu, taonani, pamaso pa Mulungu sindinama ine.
21 Pamenepo ndinadza ku mbali za Suriya ndi Kilikiya.
22 Koma ndinali wosadziwika nkhope yanga kwa Mipingo ya ku Yudeya ya mwa Kristu;
23 koma analinkumva kokha, kuti, iye wakutilondalonda ife kale, tsopane alalikira cikhulupiriroco ada cipasula kale;
24 ndipo analemekeza Mulungu mwaine.