20 Koma nkhoswe siiri ya mmodzi; koma Mulungu ali mmodzi.
21 Pamenepo kodi cilamulo citsutsana nao malonjezano a Mulungu? Msatero ai. Pakuti cikadapatsidwa cilamulo eakukhoza kucitira moyo, cilungamo cikadacokera ndithu kulamulo.
22 Komatu lembo Iinatsekereza zonse pansi pa ucimo, kuti lonjezano la kwa cikhulupiriro ca Yesu Kristu likapatsidwe kwa okhulupirirawo.
23 Koma cisanadze cikhulupiriro tinasungidwa pomvera lamulo otsekedwa kufikira cikhulupiriro cimene cikabvumbulutsidwa bwino bwino.
24 1 Momwemo cilamulo cidakhala namkungwi wathu wakutifikitsa kwa Kristu, 2 kuti tikayesedwe olungama ndi cikhulupiriro.
25 Koma popeza cadza cikhulupiriro, sitikhalanso omvera namkungwi.
26 3 Pakuti inu nonse muli ana a Mulungu, mwa cikhulupiriro ca mwa Yesu Kristu.