2 komatu ali wakumvera omsungira ndi adindo, kufikira nthawi yoikika kale ndi atate wace.
3 Koteronso ife, pamene tinali akhanda, tinali akapolo akumvera miyambo ya dziko lapansi;
4 koma pokwaniridwa nthawi, Mulungu anatuma Mwana wace, wobadwa ndi mkazi, wobadwa wakumvera lamulo,
5 kuti akaombole iwo akumvera lamulo, kuti ife tikalandire umwana.
6 Ndipo popeza muli ana, Mulungu anatumiza Mzimu wa Mwana wace alowe m'mitima yathu, wopfuula Abba, Atate.
7 Kotero kuti sulinso kapolo, koma mwana; koma ngati mwana, wolowa nyumbanso mwa Mulungu.
8 Komatu pajapo, posadziwa Mulungu inu, munacitira ukapolo iyo yosakhalamilungu m'cibadwidwe cao;