8 Komatu pajapo, posadziwa Mulungu inu, munacitira ukapolo iyo yosakhalamilungu m'cibadwidwe cao;
9 koma tsopano, podziwa Mulungu inu, koma makamaka podziwika ndi Mulungu, mubwereranso bwanji kutsata miyambo yofoka ndi yaumphawi, imene mufuna kubwerezanso kuicitira ukapolo?
10 Musunga masiku, ndi miyezi, ndi nyengo, ndi zaka.
11 Ndiopera inu, kuti kapena odadzibvutitsa ndi inu cabe.
12 Abale, ndikupemphani, khalani monga ine, pakuti inenso ndiri mongainu. Simunandicitira coipa ine;
13 koma mudziwa kuti m'kufoka kwa thupi ndinakulalikirani Uthenga Wabwino poyamba:
14 ndipo cija ca m'thupi langa cakukuyesani inu simunacipeputsa, kapena sicinakunyansirani, komatu munandilandira ine monga mngelo wa Mulungu, monga Kristu Yesu mwini.